Main pages

Surah Al-Kauther ( A River in Paradise)

Chewa

Surah Al-Kauther ( A River in Paradise) - Aya count 3

إِنَّآ أَعْطَيْنَٰكَ ٱلْكَوْثَرَ ﴿١﴾

Ndithu takupatsa zabwino zambiri (zina mwa izo ndi mtsinje wotchedwa Kauthar).[490]

فَصَلِّ لِرَبِّكَ وَٱنْحَرْ ﴿٢﴾

(Pakuti ndakupatsa zimenezo), pitiriza kupembedza Mbuye wako (moyera mtima) ndipo ipha nsembe yako (chifukwa chakuthokoza Allah pa zimene wakupatsa, monga ulemelero ndikukusankhira zabwino zambiri).[491]

إِنَّ شَانِئَكَ هُوَ ٱلْأَبْتَرُ ﴿٣﴾

Ndithu mdani wako ndiye ali wopanda mwawi. [492]