Chewa
Surah An-Nas ( Mankind ) - Aya count 6
قُلْ أَعُوذُ بِرَبِّ ٱلنَّاسِ ﴿١﴾
Nena: “Ndikudzitchinjiriza ndi Mbuye (Mleri) wa anthu (Yemwe akulinganiza zinthu zawo).[503]
مَلِكِ ٱلنَّاسِ ﴿٢﴾
Mfumu ya anthu ( Imene iri ndi mphamvu yochita chirichonse pa iwo).
مِن شَرِّ ٱلْوَسْوَاسِ ٱلْخَنَّاسِ ﴿٤﴾
Kuzoipa za mnong’onezi (yemwe amathira unong’onezi wake m’mitimaya anthu) yemwenso amabisala (posiya unong’onezi wake ngati mwini mtimawo atankumbukira Allah).[504]
ٱلَّذِى يُوَسْوِسُ فِى صُدُورِ ٱلنَّاسِ ﴿٥﴾
Yemwe amanong’oneza mzifuwa za anthu.
مِنَ ٱلْجِنَّةِ وَٱلنَّاسِ ﴿٦﴾
Wochokera m’ziwanda ndi mwa anthu.”[505]